Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 22:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Minga ndi misampha iri m'njira ya wokhota;Koma wosunga moyo wace adzatarikira imeneyo.

6. Phunzitsa mwana poyamba njira yace;Ndipo angakhale atakalamba sadzacokamo.

7. Wolemera alamulira osauka;Ndipo wokongola ndiye kapolo wa womkongoletsa.

8. Wofesa zosalungama adzakolola tsoka;Ndipo ntyole ya mkwiyo wace idzalephera.

9. Mwini diso lamataya adzadala;Pakuti apatsa osauka zakudya zace.

10. Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka;Makani ndi manyazi adzalekeka.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 22