Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 22:4-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Mphotho ya cifatso ndi kuopa, YehovaNdiye cuma, ndi ulemu, ndi moyo.

5. Minga ndi misampha iri m'njira ya wokhota;Koma wosunga moyo wace adzatarikira imeneyo.

6. Phunzitsa mwana poyamba njira yace;Ndipo angakhale atakalamba sadzacokamo.

7. Wolemera alamulira osauka;Ndipo wokongola ndiye kapolo wa womkongoletsa.

8. Wofesa zosalungama adzakolola tsoka;Ndipo ntyole ya mkwiyo wace idzalephera.

9. Mwini diso lamataya adzadala;Pakuti apatsa osauka zakudya zace.

10. Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka;Makani ndi manyazi adzalekeka.

11. Wokonda kuyera mtima,Mfumu idzakhala bwenzi lace cifukwa ca cisomo ca milomo yace.

12. Maso a Yehova acinjiriza wodziwa;Koma agwetsa mau a munthu wa ziwembu.

13. Waulesi ati, Pali mkango panjapo,Ndidzaphedwa pamakwalalapo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 22