19. Ndakudziwitsa amenewo lero, ngakhale iwedi,Kuti ukhulupirire Yehova.
20. Kodi sindinakulembera zoposa Za uphungu ndi nzeru;
21. Kuti ukadziwitse ntheradi yace ya mau oona,Nukabwere ndi mau oona kwa iwo amene anakutumiza?
22. Usalande za waumphawi cifukwa ali waumphawi,Ngakhale kutsendereza wosauka kubwalo.
23. Pakuti Yehova adzanenera mlandu wao;Omwe akwatula zao Iye adzakwatula moyo wao.
24. Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga;Ngakhale kupita ndi mwamuna waukali;
25. Kuti ungaphunzire mayendedwe ace,Ndi kutengera moyo wako msampha,
26. Usakhale wodulirana mpherere,Ngakhale kumperekera cikole ca ngongole zace.
27. Ngati ulibe cobwezeraKodi acotserenji kama lako pansi pako?