12. Maso a Yehova acinjiriza wodziwa;Koma agwetsa mau a munthu wa ziwembu.
13. Waulesi ati, Pali mkango panjapo,Ndidzaphedwa pamakwalalapo.
14. M'kamwa mwa mkazi waciwerewere muli dzenje lakuya;Yemwe Yehova amkwiyira adzagwamo.
15. Utsiru umangidwa mumtima mwa mwana;Koma ntyole yomlangira idzauingitsira kutari.
16. Wotsendereza waumphawi kuti acurukitse cuma cace,Ndi wopatsa wolemera kanthu, angosauka.
17. Chera makutu ako, numvere mau a anzeru,Nulozetse mtima wako kukadziwa zanga.