Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 22:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mbiri yabwino ifunika kopambana cuma cambiri;Kukukomera mtima anzako kuposa siliva ndi golidi.

2. Wolemera ndi wosauka akumana,Wolenga onsewo ndiye Yehova.

3. Wocenjera aona zoipa, nabisala;Koma acibwana angopitirira, nalipitsidwa.

4. Mphotho ya cifatso ndi kuopa, YehovaNdiye cuma, ndi ulemu, ndi moyo.

5. Minga ndi misampha iri m'njira ya wokhota;Koma wosunga moyo wace adzatarikira imeneyo.

6. Phunzitsa mwana poyamba njira yace;Ndipo angakhale atakalamba sadzacokamo.

7. Wolemera alamulira osauka;Ndipo wokongola ndiye kapolo wa womkongoletsa.

8. Wofesa zosalungama adzakolola tsoka;Ndipo ntyole ya mkwiyo wace idzalephera.

9. Mwini diso lamataya adzadala;Pakuti apatsa osauka zakudya zace.

10. Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka;Makani ndi manyazi adzalekeka.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 22