Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 21:26-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ena asirira modukidwa tsiku lonse;Koma wolungama amapatsa osamana.

27. Nsembe ya oipa inyansa;Makamaka pakudza nayo iwo mwaciwembu.

28. Mboni yonama idzafa;Koma mwamuna wakumvetsa adzanena mosakayika,

29. Munthu woipa aumitsa nkhope yace;Koma woongoka mtima akonza njira zace.

30. Kulibe nzeru ngakhale lunthaNgakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.

31. Kavalo amakonzedweratu cifukwa ca tsiku la nkhondo;Koma wopulumutsa ndiye Yehova.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 21