Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 21:22-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Wanzeru akwera pa mudzi wa olimba,Nagwetsa mphamvu yace imene anaikhulupirira.

23. Wosunga m'kamwa mwace ndi lilime laceAsunga moyo wace kumabvuto.

24. Wonyada wodzikuza dzina lace ndiye wonyoza;Acita mwaukali modzitama.

25. Cifuniro ca wolesi cimupha;Cifukwa manja ace akana kugwira nchito.

26. Ena asirira modukidwa tsiku lonse;Koma wolungama amapatsa osamana.

27. Nsembe ya oipa inyansa;Makamaka pakudza nayo iwo mwaciwembu.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 21