22. Wanzeru akwera pa mudzi wa olimba,Nagwetsa mphamvu yace imene anaikhulupirira.
23. Wosunga m'kamwa mwace ndi lilime laceAsunga moyo wace kumabvuto.
24. Wonyada wodzikuza dzina lace ndiye wonyoza;Acita mwaukali modzitama.
25. Cifuniro ca wolesi cimupha;Cifukwa manja ace akana kugwira nchito.
26. Ena asirira modukidwa tsiku lonse;Koma wolungama amapatsa osamana.
27. Nsembe ya oipa inyansa;Makamaka pakudza nayo iwo mwaciwembu.