Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 21:13-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Wotseka makutu ace polira waumphawi,Nayenso adzalira koma osamvedwa.

14. Mphatso ya m'tseri ipembedza mkwiyo,Ndi mtulo wa pamfunga ukali wolimba.

15. Kucita ciweruzo kukondweretsa wolungama;Koma kuwaononga akucita mphulupulu,

16. Munthu wosocera pa njira ya nzeruAdzakhala m'msonkhano wa akufa.

17. Wokonda zoseketsa adzasauka;Wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.

18. Wocimwa ndiye ciombolo ca wolungama;Ndipo waciwembu adzalowa m'malo mwa oongoka mtima.

19. Kukhala m'cipululu kufunikaKuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wong'ung'udza.

20. Mokhala wanzeru muli katundu wofunika ndi mafuta;Koma wopusa angozimeza.

21. Wolondola cilungamo ndi cifundoApeza moyo, ndi cilungamo, ndi ulemu.

22. Wanzeru akwera pa mudzi wa olimba,Nagwetsa mphamvu yace imene anaikhulupirira.

23. Wosunga m'kamwa mwace ndi lilime laceAsunga moyo wace kumabvuto.

24. Wonyada wodzikuza dzina lace ndiye wonyoza;Acita mwaukali modzitama.

25. Cifuniro ca wolesi cimupha;Cifukwa manja ace akana kugwira nchito.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 21