13. Wotseka makutu ace polira waumphawi,Nayenso adzalira koma osamvedwa.
14. Mphatso ya m'tseri ipembedza mkwiyo,Ndi mtulo wa pamfunga ukali wolimba.
15. Kucita ciweruzo kukondweretsa wolungama;Koma kuwaononga akucita mphulupulu,
16. Munthu wosocera pa njira ya nzeruAdzakhala m'msonkhano wa akufa.
17. Wokonda zoseketsa adzasauka;Wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
18. Wocimwa ndiye ciombolo ca wolungama;Ndipo waciwembu adzalowa m'malo mwa oongoka mtima.
19. Kukhala m'cipululu kufunikaKuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wong'ung'udza.
20. Mokhala wanzeru muli katundu wofunika ndi mafuta;Koma wopusa angozimeza.
21. Wolondola cilungamo ndi cifundoApeza moyo, ndi cilungamo, ndi ulemu.
22. Wanzeru akwera pa mudzi wa olimba,Nagwetsa mphamvu yace imene anaikhulupirira.