Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 21:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mtima wa mfumu uli m'dzanja la Yehova ngati mitsinje ya madzi;Aulozetsa komwe afuna.

2. Njira zonse za munthu zilungama pamaso pace;Koma Yehova ayesa mitima.

3. Kucita cilungamo ndi ciweruzoKupambana ndi nsembe kumkonda Yehova.

4. Maso akunyada, ndi mtima wodzikuza,Ndi nyali ya oipa, ziri cimo.

5. Zoganizira za wakhama zicurukitsadi katundu;Koma yense wansontho angopeza umphawi.

6. Kupata cuma ndi lilime lonama ndiko nkhungu yoyendayenda, ngakhale misampha ya imfa.

7. Ciwawa ca amphulupulu cidzawakokolola;Cifukwa akana kucita ciweruzo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 21