Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 21:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mtima wa mfumu uli m'dzanja la Yehova ngati mitsinje ya madzi;Aulozetsa komwe afuna.

2. Njira zonse za munthu zilungama pamaso pace;Koma Yehova ayesa mitima.

3. Kucita cilungamo ndi ciweruzoKupambana ndi nsembe kumkonda Yehova.

4. Maso akunyada, ndi mtima wodzikuza,Ndi nyali ya oipa, ziri cimo.

5. Zoganizira za wakhama zicurukitsadi katundu;Koma yense wansontho angopeza umphawi.

6. Kupata cuma ndi lilime lonama ndiko nkhungu yoyendayenda, ngakhale misampha ya imfa.

7. Ciwawa ca amphulupulu cidzawakokolola;Cifukwa akana kucita ciweruzo.

8. Wosenza cimo njira yace ikhotakhota;Koma nchito ya woyera mtima ilungama.

9. Kukhala pa ngondya ya tsindwi kufunikaKuposa kukhala m'nyumba ndi mkazi wolongolola.

10. Wamphulupulu mtima wace umkhumba zoipa;Sakomera mtima mnzace.

11. Polangidwa wonyoza, wacibwana alandira nzeru,Naphunzira pakuyang'ana pa wanzeru.

12. Wolungama aganizira za nyumba ya wamphulupulu,Kuti amphulupulu amagwetsedwa, naona zoipa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 21