Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 20:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Wolungama woyenda mwangwiro,Anace adala pambuyo pace.

8. Mfumu yokhala pa mpando waweruziraIpitikitsa zoipa zonse ndi maso ace.

9. Ndani anganene, Ndasambitsa mtima wanga,Ndayera opanda cimo?

10. Miyeso yosiyana, ndi malicero osiyana,Zonse ziwirizi zinyansa Yehova.

11. Ngakhale mwana adziwika ndi nchito zace;Ngati nchito yace iri yoyera ngakhale yolungama.

12. Khutu lakumva, ndi diso lopenya,Yehova anapanga onse awiriwo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 20