Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 20:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Wolesi salima cifukwa ca cisanu;Adzapemphapempha m'masika osalandira kanthu.

5. Uphungu wa m'mtima mwa munthu ndiwo madzi akuya;Koma munthu wozindikira adzatungapo,

6. Anthu ambiri abukitsa yense kukoma mtima kwace;Koma ndani angapeze munthu wokhulupirika?

7. Wolungama woyenda mwangwiro,Anace adala pambuyo pace.

8. Mfumu yokhala pa mpando waweruziraIpitikitsa zoipa zonse ndi maso ace.

9. Ndani anganene, Ndasambitsa mtima wanga,Ndayera opanda cimo?

10. Miyeso yosiyana, ndi malicero osiyana,Zonse ziwirizi zinyansa Yehova.

11. Ngakhale mwana adziwika ndi nchito zace;Ngati nchito yace iri yoyera ngakhale yolungama.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 20