Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 20:3-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Kuli ulemu kwa mwamuna kupewa ndeu;Koma zitsiru zonse zimangokangana,

4. Wolesi salima cifukwa ca cisanu;Adzapemphapempha m'masika osalandira kanthu.

5. Uphungu wa m'mtima mwa munthu ndiwo madzi akuya;Koma munthu wozindikira adzatungapo,

6. Anthu ambiri abukitsa yense kukoma mtima kwace;Koma ndani angapeze munthu wokhulupirika?

7. Wolungama woyenda mwangwiro,Anace adala pambuyo pace.

8. Mfumu yokhala pa mpando waweruziraIpitikitsa zoipa zonse ndi maso ace.

9. Ndani anganene, Ndasambitsa mtima wanga,Ndayera opanda cimo?

10. Miyeso yosiyana, ndi malicero osiyana,Zonse ziwirizi zinyansa Yehova.

11. Ngakhale mwana adziwika ndi nchito zace;Ngati nchito yace iri yoyera ngakhale yolungama.

12. Khutu lakumva, ndi diso lopenya,Yehova anapanga onse awiriwo.

13. Usakonde tulo ungasauke;Phenyula maso, udzakhuta zakudya.

14. Wogula ati, Cacabe cimeneco.Koma atacoka adzitama.

15. Alipo golidi ndi ngale zambiri;Koma milomo yodziwa ndiyo cokometsera ca mtengo wapatari.

16. Tenga maraya a woperekera mlendo cikole;Woperekera mkazi wacilendo cikole umgwire mwini.

17. Zakudya za cinyengo zikondweretsa munthu;Koma pambuyo pace m'kamwa mwace mudzadzala tinsangalabwi.

18. Uphungu utsimikiza zolingalira,Ponya nkhondo utapanga upo.

19. Kazitape woyendayenda awanditsa zinsinsi;Usadudukire woyasama milomo yace.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 20