Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 20:24-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Yehova alongosola mayendedwe a mwamuna;Munthu tsono angazindikire bwanji njira yace?

25. Kunena mwansontho, ici ncopatulika, kuli msampha kwa munthu,Ndi kusinkhasinkha pambuyo pace atawinda.

26. Mfumu yanzeru ipeta amphulupulu,Niyendetsapo njinga ya gareta.

27. Mzimu wa munthu ndiwo nyali ya Yehova;Usanthula m'kati monse mwa mimba.

28. Cifundo ndi ntheradi zisunga mfumu;Cifundo cicirikiza mpando wace.

29. Ulemerero wa anyamata ndiwo mphamvu yao;Kukongola kwa nkhalamba ndi

30. Mikwingwirima yopweteka icotsa zoipa;Ndi mikwapulo ilowa m'kati mwa mimba.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 20