Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 20:21-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Colowa cingalandiridwe msanga msanga poyamba pace;Koma citsiriziro cace sicidzadala.

22. Usanene, Ndidzabwezera zoipa;Yembekeza Yehova, adzakupulumutsa.

23. Miyeso yosiyana inyansa Yehova,Ndi mulingo wonyenga suli wabwino.

24. Yehova alongosola mayendedwe a mwamuna;Munthu tsono angazindikire bwanji njira yace?

25. Kunena mwansontho, ici ncopatulika, kuli msampha kwa munthu,Ndi kusinkhasinkha pambuyo pace atawinda.

26. Mfumu yanzeru ipeta amphulupulu,Niyendetsapo njinga ya gareta.

27. Mzimu wa munthu ndiwo nyali ya Yehova;Usanthula m'kati monse mwa mimba.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 20