17. Zakudya za cinyengo zikondweretsa munthu;Koma pambuyo pace m'kamwa mwace mudzadzala tinsangalabwi.
18. Uphungu utsimikiza zolingalira,Ponya nkhondo utapanga upo.
19. Kazitape woyendayenda awanditsa zinsinsi;Usadudukire woyasama milomo yace.
20. Wotemberera atate wace ndi, amace,Nyali yace idzazima mu mdima woti bi.
21. Colowa cingalandiridwe msanga msanga poyamba pace;Koma citsiriziro cace sicidzadala.
22. Usanene, Ndidzabwezera zoipa;Yembekeza Yehova, adzakupulumutsa.
23. Miyeso yosiyana inyansa Yehova,Ndi mulingo wonyenga suli wabwino.
24. Yehova alongosola mayendedwe a mwamuna;Munthu tsono angazindikire bwanji njira yace?
25. Kunena mwansontho, ici ncopatulika, kuli msampha kwa munthu,Ndi kusinkhasinkha pambuyo pace atawinda.
26. Mfumu yanzeru ipeta amphulupulu,Niyendetsapo njinga ya gareta.