Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 20:17-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Zakudya za cinyengo zikondweretsa munthu;Koma pambuyo pace m'kamwa mwace mudzadzala tinsangalabwi.

18. Uphungu utsimikiza zolingalira,Ponya nkhondo utapanga upo.

19. Kazitape woyendayenda awanditsa zinsinsi;Usadudukire woyasama milomo yace.

20. Wotemberera atate wace ndi, amace,Nyali yace idzazima mu mdima woti bi.

21. Colowa cingalandiridwe msanga msanga poyamba pace;Koma citsiriziro cace sicidzadala.

22. Usanene, Ndidzabwezera zoipa;Yembekeza Yehova, adzakupulumutsa.

23. Miyeso yosiyana inyansa Yehova,Ndi mulingo wonyenga suli wabwino.

24. Yehova alongosola mayendedwe a mwamuna;Munthu tsono angazindikire bwanji njira yace?

25. Kunena mwansontho, ici ncopatulika, kuli msampha kwa munthu,Ndi kusinkhasinkha pambuyo pace atawinda.

26. Mfumu yanzeru ipeta amphulupulu,Niyendetsapo njinga ya gareta.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 20