1. Vinyo acita ciphwete, cakumwa caukali cisokosa;Wosocera nazo alibe nzeru.
2. Kuopsya kwa mfumu ndiko kubangula kwa mkango;Womputa acimwira moyo wace wace.
3. Kuli ulemu kwa mwamuna kupewa ndeu;Koma zitsiru zonse zimangokangana,
4. Wolesi salima cifukwa ca cisanu;Adzapemphapempha m'masika osalandira kanthu.
5. Uphungu wa m'mtima mwa munthu ndiwo madzi akuya;Koma munthu wozindikira adzatungapo,
6. Anthu ambiri abukitsa yense kukoma mtima kwace;Koma ndani angapeze munthu wokhulupirika?
7. Wolungama woyenda mwangwiro,Anace adala pambuyo pace.