Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 19:6-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ambiri adzapembedza waufulu;Ndipo yense ndi bwenzi la munthu wopatsa.

7. Abale onse a wosauka amuda;Nanga mabwenzi ace kodi satanimphirana naye?Awatsata ndi mau, koma kuli zi.

8. Wolandira nzeru akonda moyo wace;Wosunga luntha adzapeza zabwino.

9. Mboni yonama sidzapulumuka cilango;Wolankhula mabodza adzaonongeka.

10. Wopusa sayenera kukhala ndi zinthu zolongosoka;Nanga kapolo ayenera kulamulira akalonga kodi?

11. Kulingalira kwa munthu kucedwetsa mkwiyo;Ulemerero wace uli wakuti akhululukire colakwa.

12. Mkwiyo wa mfumu ukunga kubangula kwa mkango;Koma kukoma mtima kwace kunga mame pamsipu.

13. Mwana wopusa ndiye tsoka la atate wace;Ndipo makangano a mkazi ndiwo kudontha-donthabe.

14. Nyumba ndi cuma ndizo colowa ca atate;Koma mkazi wanzeru acokera kwa Yehova.

15. Ulesi ugonetsa tulo tofa nato;Ndipo moyo wamkhongono udzamva njala.

16. Wosunga lamulo asunga moyo wace;Wonyalanyaza mayendedwe ace adzafa.

17. Wocitira waumphawi cifundo abwereka Yehova;Adzambwezera cokoma caceco.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 19