4. Cuma cionjezetsa mabwenzi ambiri;Koma mnzace wa waumphawi amleka.
5. Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa;Wolankhula mabodza sadzapulumuka.
6. Ambiri adzapembedza waufulu;Ndipo yense ndi bwenzi la munthu wopatsa.
7. Abale onse a wosauka amuda;Nanga mabwenzi ace kodi satanimphirana naye?Awatsata ndi mau, koma kuli zi.
8. Wolandira nzeru akonda moyo wace;Wosunga luntha adzapeza zabwino.
9. Mboni yonama sidzapulumuka cilango;Wolankhula mabodza adzaonongeka.
10. Wopusa sayenera kukhala ndi zinthu zolongosoka;Nanga kapolo ayenera kulamulira akalonga kodi?
11. Kulingalira kwa munthu kucedwetsa mkwiyo;Ulemerero wace uli wakuti akhululukire colakwa.
12. Mkwiyo wa mfumu ukunga kubangula kwa mkango;Koma kukoma mtima kwace kunga mame pamsipu.
13. Mwana wopusa ndiye tsoka la atate wace;Ndipo makangano a mkazi ndiwo kudontha-donthabe.
14. Nyumba ndi cuma ndizo colowa ca atate;Koma mkazi wanzeru acokera kwa Yehova.
15. Ulesi ugonetsa tulo tofa nato;Ndipo moyo wamkhongono udzamva njala.
16. Wosunga lamulo asunga moyo wace;Wonyalanyaza mayendedwe ace adzafa.
17. Wocitira waumphawi cifundo abwereka Yehova;Adzambwezera cokoma caceco.
18. Menya mwanako, ciyembekezero ciripo,Osafunitsa kumuononga.
19. Munthu waukali alipire mwini;Pakuti ukampulumutsa udzateronso.
20. Tamvera uphungu, nulandire mwambo,Kuti ukhale wanzeru pa cimariziro cako,
21. Muli zolingalira zambiri m'mtima mwa munthu;Koma uphungu wa Yehova ndiwo udzaimika.
22. Cotikondetsa munthu ndico kukoma mtima kwace;Ndipo wosauka apambana munthu wonama.