Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 19:4-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Cuma cionjezetsa mabwenzi ambiri;Koma mnzace wa waumphawi amleka.

5. Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa;Wolankhula mabodza sadzapulumuka.

6. Ambiri adzapembedza waufulu;Ndipo yense ndi bwenzi la munthu wopatsa.

7. Abale onse a wosauka amuda;Nanga mabwenzi ace kodi satanimphirana naye?Awatsata ndi mau, koma kuli zi.

8. Wolandira nzeru akonda moyo wace;Wosunga luntha adzapeza zabwino.

9. Mboni yonama sidzapulumuka cilango;Wolankhula mabodza adzaonongeka.

10. Wopusa sayenera kukhala ndi zinthu zolongosoka;Nanga kapolo ayenera kulamulira akalonga kodi?

11. Kulingalira kwa munthu kucedwetsa mkwiyo;Ulemerero wace uli wakuti akhululukire colakwa.

12. Mkwiyo wa mfumu ukunga kubangula kwa mkango;Koma kukoma mtima kwace kunga mame pamsipu.

13. Mwana wopusa ndiye tsoka la atate wace;Ndipo makangano a mkazi ndiwo kudontha-donthabe.

14. Nyumba ndi cuma ndizo colowa ca atate;Koma mkazi wanzeru acokera kwa Yehova.

15. Ulesi ugonetsa tulo tofa nato;Ndipo moyo wamkhongono udzamva njala.

16. Wosunga lamulo asunga moyo wace;Wonyalanyaza mayendedwe ace adzafa.

17. Wocitira waumphawi cifundo abwereka Yehova;Adzambwezera cokoma caceco.

18. Menya mwanako, ciyembekezero ciripo,Osafunitsa kumuononga.

19. Munthu waukali alipire mwini;Pakuti ukampulumutsa udzateronso.

20. Tamvera uphungu, nulandire mwambo,Kuti ukhale wanzeru pa cimariziro cako,

21. Muli zolingalira zambiri m'mtima mwa munthu;Koma uphungu wa Yehova ndiwo udzaimika.

22. Cotikondetsa munthu ndico kukoma mtima kwace;Ndipo wosauka apambana munthu wonama.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 19