2. Kukhumba kosadziwa sikuli kwabwino;Ndipo wofulumira ndi mapazi ace amacimwa.
3. Utsiru wa munthu ukhotetsa njira yace;Mtima wace udandaula pa Yehova.
4. Cuma cionjezetsa mabwenzi ambiri;Koma mnzace wa waumphawi amleka.
5. Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa;Wolankhula mabodza sadzapulumuka.
6. Ambiri adzapembedza waufulu;Ndipo yense ndi bwenzi la munthu wopatsa.