16. Wosunga lamulo asunga moyo wace;Wonyalanyaza mayendedwe ace adzafa.
17. Wocitira waumphawi cifundo abwereka Yehova;Adzambwezera cokoma caceco.
18. Menya mwanako, ciyembekezero ciripo,Osafunitsa kumuononga.
19. Munthu waukali alipire mwini;Pakuti ukampulumutsa udzateronso.
20. Tamvera uphungu, nulandire mwambo,Kuti ukhale wanzeru pa cimariziro cako,
21. Muli zolingalira zambiri m'mtima mwa munthu;Koma uphungu wa Yehova ndiwo udzaimika.
22. Cotikondetsa munthu ndico kukoma mtima kwace;Ndipo wosauka apambana munthu wonama.
23. Kuopa Yehova kupatsa moyo;Wokhala nako adzakhala wokhuta;Zoipa sizidzamgwera.