Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 19:16-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Wosunga lamulo asunga moyo wace;Wonyalanyaza mayendedwe ace adzafa.

17. Wocitira waumphawi cifundo abwereka Yehova;Adzambwezera cokoma caceco.

18. Menya mwanako, ciyembekezero ciripo,Osafunitsa kumuononga.

19. Munthu waukali alipire mwini;Pakuti ukampulumutsa udzateronso.

20. Tamvera uphungu, nulandire mwambo,Kuti ukhale wanzeru pa cimariziro cako,

21. Muli zolingalira zambiri m'mtima mwa munthu;Koma uphungu wa Yehova ndiwo udzaimika.

22. Cotikondetsa munthu ndico kukoma mtima kwace;Ndipo wosauka apambana munthu wonama.

23. Kuopa Yehova kupatsa moyo;Wokhala nako adzakhala wokhuta;Zoipa sizidzamgwera.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 19