Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 19:12-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Mkwiyo wa mfumu ukunga kubangula kwa mkango;Koma kukoma mtima kwace kunga mame pamsipu.

13. Mwana wopusa ndiye tsoka la atate wace;Ndipo makangano a mkazi ndiwo kudontha-donthabe.

14. Nyumba ndi cuma ndizo colowa ca atate;Koma mkazi wanzeru acokera kwa Yehova.

15. Ulesi ugonetsa tulo tofa nato;Ndipo moyo wamkhongono udzamva njala.

16. Wosunga lamulo asunga moyo wace;Wonyalanyaza mayendedwe ace adzafa.

17. Wocitira waumphawi cifundo abwereka Yehova;Adzambwezera cokoma caceco.

18. Menya mwanako, ciyembekezero ciripo,Osafunitsa kumuononga.

19. Munthu waukali alipire mwini;Pakuti ukampulumutsa udzateronso.

20. Tamvera uphungu, nulandire mwambo,Kuti ukhale wanzeru pa cimariziro cako,

21. Muli zolingalira zambiri m'mtima mwa munthu;Koma uphungu wa Yehova ndiwo udzaimika.

22. Cotikondetsa munthu ndico kukoma mtima kwace;Ndipo wosauka apambana munthu wonama.

23. Kuopa Yehova kupatsa moyo;Wokhala nako adzakhala wokhuta;Zoipa sizidzamgwera.

24. Wolesi alonga dzanja lace m'mbale,Osalibwezanso kukamwa kwace.

25. Menya wonyoza, ndipo acibwana adzaceniera;Nudzudzule wozindikira adzazindikira nzeru.

26. Wolanda za atate, ndi wopitikitsa amai,Ndiye mwana wocititsa manyazi ndi wogwetsa nkhope.

27. Ukangofuna, mwananga, kusocera kusiya mau akudziwitsa,Leka kumva mwambo.

28. Mboni yopanda pace inyoza ciweruzo;M'kamwa mwa amphulupulu mumeza zoipa,

Werengani mutu wathunthu Miyambi 19