Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 19:12-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Mkwiyo wa mfumu ukunga kubangula kwa mkango;Koma kukoma mtima kwace kunga mame pamsipu.

13. Mwana wopusa ndiye tsoka la atate wace;Ndipo makangano a mkazi ndiwo kudontha-donthabe.

14. Nyumba ndi cuma ndizo colowa ca atate;Koma mkazi wanzeru acokera kwa Yehova.

15. Ulesi ugonetsa tulo tofa nato;Ndipo moyo wamkhongono udzamva njala.

16. Wosunga lamulo asunga moyo wace;Wonyalanyaza mayendedwe ace adzafa.

17. Wocitira waumphawi cifundo abwereka Yehova;Adzambwezera cokoma caceco.

18. Menya mwanako, ciyembekezero ciripo,Osafunitsa kumuononga.

19. Munthu waukali alipire mwini;Pakuti ukampulumutsa udzateronso.

20. Tamvera uphungu, nulandire mwambo,Kuti ukhale wanzeru pa cimariziro cako,

Werengani mutu wathunthu Miyambi 19