1. Wosauka woyenda mwangwiroAposa wokhetsa milomo ndi wopusa.
2. Kukhumba kosadziwa sikuli kwabwino;Ndipo wofulumira ndi mapazi ace amacimwa.
3. Utsiru wa munthu ukhotetsa njira yace;Mtima wace udandaula pa Yehova.
4. Cuma cionjezetsa mabwenzi ambiri;Koma mnzace wa waumphawi amleka.
5. Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa;Wolankhula mabodza sadzapulumuka.
6. Ambiri adzapembedza waufulu;Ndipo yense ndi bwenzi la munthu wopatsa.
7. Abale onse a wosauka amuda;Nanga mabwenzi ace kodi satanimphirana naye?Awatsata ndi mau, koma kuli zi.
8. Wolandira nzeru akonda moyo wace;Wosunga luntha adzapeza zabwino.
9. Mboni yonama sidzapulumuka cilango;Wolankhula mabodza adzaonongeka.
10. Wopusa sayenera kukhala ndi zinthu zolongosoka;Nanga kapolo ayenera kulamulira akalonga kodi?