Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 17:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Wobisa colakwa afunitsa cikondano;Koma wobwereza-bwereza mau afetsa ubwenzi.

10. Cidzudzulo cilowa m'kati mwa wozindikira,Kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.

11. Woipa amafuna kupanduka kokha;Koma adzamtumizira mthenga wankhanza.

12. Kukomana ndi citsiru m'kupusa kwaceKuopsya koposa cirombo cocicotsera anace.

13. Wobwezera zabwino zoipa,Zoipa sizidzamcokera kwao.

14. Ciyambi ca ndeu cifanana ndi kutsegulira madzi;Tsono kupikisana kusanayambe tasiya makani.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 17