Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 17:5-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Wocitira ciphwete aumphawi atonza Mlengi;Wokondwera ndi tsoka sadzapulumuka cilango.

6. Zidzukulu ndizo korona wa okalamba;Ndipo ulemerero wa ana ndiwo atate ao.

7. Mlomo wangwiro suyenera citsiru;Ngakhale mlomo wonama suyenera kalonga ndi pang'ono ponse.

8. Wolandira cokometsera mlandu aciyesa ngale;Pali ponse popita iye acenjera.

9. Wobisa colakwa afunitsa cikondano;Koma wobwereza-bwereza mau afetsa ubwenzi.

10. Cidzudzulo cilowa m'kati mwa wozindikira,Kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.

11. Woipa amafuna kupanduka kokha;Koma adzamtumizira mthenga wankhanza.

12. Kukomana ndi citsiru m'kupusa kwaceKuopsya koposa cirombo cocicotsera anace.

13. Wobwezera zabwino zoipa,Zoipa sizidzamcokera kwao.

14. Ciyambi ca ndeu cifanana ndi kutsegulira madzi;Tsono kupikisana kusanayambe tasiya makani.

15. Wokometsa mlandu wa wamphulupulu, ndi wotsutsa wolungama,Onse awiriwa amnyansa Yehova.

16. Kodi bwanji mtengo wogulira nzeru uli m'dzanja la citsiru,Popeza wopusa alibe mtima?

17. Bwenzi limakonda nthawi zonse;Ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

18. Munthu wosowa nzeru apangana kulipirira wina,Napereka cikole pamaso pa mnzace.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 17