Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 17:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Wobala citsiru adzicititsa cisoni;Ndipo atate wa wopusa sakondwa.

22. Mtima wosekerera uciritsa bwinoKoma mzimu wosweka uphwetsa mafupa,

23. Munthu woipa alandira cokometsera mlandu coturutsa m'mfunga,Kuti apambukitse mayendedwe a ciweruzo.

24. Nzeru iri pamaso pa wozindikira;Koma maso a wopusa ali m'malekezero a dziko.

25. Mwana wopusa acititsa atate wace cisoni,Namvetsa zowawa amace wombala.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 17