Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 17:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Bwenzi limakonda nthawi zonse;Ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

18. Munthu wosowa nzeru apangana kulipirira wina,Napereka cikole pamaso pa mnzace.

19. Wokonda ndeu akonda kulakwa;Ndipo wotarikitsa khomo lace afunafuna kuonongeka.

20. Wokhota mtima sadzapeza bwinoNdipo mwini lilime lokhota adzagwa m'zoipa.

21. Wobala citsiru adzicititsa cisoni;Ndipo atate wa wopusa sakondwa.

22. Mtima wosekerera uciritsa bwinoKoma mzimu wosweka uphwetsa mafupa,

Werengani mutu wathunthu Miyambi 17