16. Kodi bwanji mtengo wogulira nzeru uli m'dzanja la citsiru,Popeza wopusa alibe mtima?
17. Bwenzi limakonda nthawi zonse;Ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.
18. Munthu wosowa nzeru apangana kulipirira wina,Napereka cikole pamaso pa mnzace.
19. Wokonda ndeu akonda kulakwa;Ndipo wotarikitsa khomo lace afunafuna kuonongeka.
20. Wokhota mtima sadzapeza bwinoNdipo mwini lilime lokhota adzagwa m'zoipa.
21. Wobala citsiru adzicititsa cisoni;Ndipo atate wa wopusa sakondwa.
22. Mtima wosekerera uciritsa bwinoKoma mzimu wosweka uphwetsa mafupa,
23. Munthu woipa alandira cokometsera mlandu coturutsa m'mfunga,Kuti apambukitse mayendedwe a ciweruzo.
24. Nzeru iri pamaso pa wozindikira;Koma maso a wopusa ali m'malekezero a dziko.
25. Mwana wopusa acititsa atate wace cisoni,Namvetsa zowawa amace wombala.
26. Kulipiritsa wolungama sikuli kwabwino,Ngakhale kukwapula akuru cifukwa aongoka mtima.