Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 17:15-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Wokometsa mlandu wa wamphulupulu, ndi wotsutsa wolungama,Onse awiriwa amnyansa Yehova.

16. Kodi bwanji mtengo wogulira nzeru uli m'dzanja la citsiru,Popeza wopusa alibe mtima?

17. Bwenzi limakonda nthawi zonse;Ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

18. Munthu wosowa nzeru apangana kulipirira wina,Napereka cikole pamaso pa mnzace.

19. Wokonda ndeu akonda kulakwa;Ndipo wotarikitsa khomo lace afunafuna kuonongeka.

20. Wokhota mtima sadzapeza bwinoNdipo mwini lilime lokhota adzagwa m'zoipa.

21. Wobala citsiru adzicititsa cisoni;Ndipo atate wa wopusa sakondwa.

22. Mtima wosekerera uciritsa bwinoKoma mzimu wosweka uphwetsa mafupa,

23. Munthu woipa alandira cokometsera mlandu coturutsa m'mfunga,Kuti apambukitse mayendedwe a ciweruzo.

24. Nzeru iri pamaso pa wozindikira;Koma maso a wopusa ali m'malekezero a dziko.

25. Mwana wopusa acititsa atate wace cisoni,Namvetsa zowawa amace wombala.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 17