1. Nyenyeswa youma, pokhala mtendere,Iposa nyumba yodzala nyama yansembe, pali makangano.
2. Kapolo wocitamwanzeruAdzalamulira mwana wocititsa manyazi,Nadzagawana nao abale colowa.
3. Siliva ali ndi mbiya yosungunulira, golidi ali ndi ng'anjo;Koma Yehova ayesa mitima.
4. Wocimwa amasamalira milomo yolakwa;Wonama amvera lilime losakaza.
5. Wocitira ciphwete aumphawi atonza Mlengi;Wokondwera ndi tsoka sadzapulumuka cilango.
6. Zidzukulu ndizo korona wa okalamba;Ndipo ulemerero wa ana ndiwo atate ao.
7. Mlomo wangwiro suyenera citsiru;Ngakhale mlomo wonama suyenera kalonga ndi pang'ono ponse.