9. Mtima wa munthu ulingalira njira yace;Koma Yehova ayendetsa mapazi ace.
10. Mau a mlauli ali m'milomo ya mfumu;M'kamwa mwace simudzacita cetera poweruza.
11. Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova;Ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m'thumba.
12. Kucita mphulupulu kunyansa mafumu;Pakuti mpando wao wakhazikika ndi cilungamo.
13. Milomo yolungama ikondweretsa mafumu;Wonena zoongoka amkonda.
14. Mkwiyo wa mfumu ndi mithenga ya imfa;Wanzeru adzaukhulula.
15. M'kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo;Kukoma mtima kwace kunga mtambo wa mvula ya masika.