Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 16:9-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Mtima wa munthu ulingalira njira yace;Koma Yehova ayendetsa mapazi ace.

10. Mau a mlauli ali m'milomo ya mfumu;M'kamwa mwace simudzacita cetera poweruza.

11. Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova;Ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m'thumba.

12. Kucita mphulupulu kunyansa mafumu;Pakuti mpando wao wakhazikika ndi cilungamo.

13. Milomo yolungama ikondweretsa mafumu;Wonena zoongoka amkonda.

14. Mkwiyo wa mfumu ndi mithenga ya imfa;Wanzeru adzaukhulula.

15. M'kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo;Kukoma mtima kwace kunga mtambo wa mvula ya masika.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 16