Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 16:11-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova;Ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m'thumba.

12. Kucita mphulupulu kunyansa mafumu;Pakuti mpando wao wakhazikika ndi cilungamo.

13. Milomo yolungama ikondweretsa mafumu;Wonena zoongoka amkonda.

14. Mkwiyo wa mfumu ndi mithenga ya imfa;Wanzeru adzaukhulula.

15. M'kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo;Kukoma mtima kwace kunga mtambo wa mvula ya masika.

16. Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golidi,Kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?

17. Khwalala la oongoka mtima ndilo lakuti asiye zoipa;Wosunga njira yace acinjiriza moyo wace.

18. Kunyada kutsogolera kuonongekaMtinia wodzikuza ndi kutsogolera kupunthwa.

19. Kufatsa mtima ndi osaukaKuposa kugawana zofunkha ndi onyada.

20. Wolabadira mau adzapeza bwino;Ndipo wokhulupirira Yehova adala.

21. Wanzeru mtima adzachedwa wocenjera;Ndipo kukoma kwa milomo kuyenjezera kuphunzira.

22. Nzeru ndi kasupe wa moyo kwa mwini wace;Koma mwambo wa zitsiru ndi utsiru.

23. Mtima wa wanzeru ucenjeza m'kamwa mwace,Nuphunzitsanso milomo yace.

24. Mau okoma ndiwo cisa ca uci,Otsekemera m'moyo ndi olamitsa mafupa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 16