9. Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;Koma wokhotetsa njira zace adzadziwika.
10. Wotsinzinira acititsa cisoni;Koma wodzudzula momveka acita mtendere.
11. M'kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;Koma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.
12. Udani upikisanitsa;Koma cikondi cikwirira zolakwa zonse.
13. Nzeru ipezedwa m'milomo ya wozindikira;Koma wopusa pamsana pace ntyole.
14. Anzeru akundika zomwe adziwaKoma m'kamwa mwa citsiru muononga tsopano lino.
15. Cuma ca wolemera ndi mudzi wace wolimba;Koma umphawi wao uononga osauka.
16. Nchito za wolungama zipatsa moyo;Koma phindu la oipa licimwitsa.
17. Wosunga mwambo ali m'njira ya moyo;Koma wosiya cidzudzulo asocera.
18. Wobisa udani ali ndi milomo yonama;Wonena ugogodi ndiye citsiru.
19. Pocuruka mau zolakwa sizisoweka;Koma wokhala cete acita mwanzeru.
20. Lilime la wolungama likunga siliva wosankhika;Koma mtima wa oipa uli wacabe.
21. Milomo ya wolungama imadyetsa ambiri;Koma zitsiru zimafa posowa nzeru.
22. Madalitso a Yehova alemeretsa,Saonjezerapo cisoni.