Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 10:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Madalitso ali pamtu pa wolungamaKoma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.

7. Amayesa wolungama wodala pamkumbukira;Koma dzina la oipa lidzabvunda.

8. Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;Koma citsiru colongolola cidzagwa.

9. Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;Koma wokhotetsa njira zace adzadziwika.

10. Wotsinzinira acititsa cisoni;Koma wodzudzula momveka acita mtendere.

11. M'kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;Koma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.

12. Udani upikisanitsa;Koma cikondi cikwirira zolakwa zonse.

13. Nzeru ipezedwa m'milomo ya wozindikira;Koma wopusa pamsana pace ntyole.

14. Anzeru akundika zomwe adziwaKoma m'kamwa mwa citsiru muononga tsopano lino.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 10