3. Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama;Koma amainga cifuniro ca wocimwa.
4. Wocita ndi dzanja laulesi amasauka;Koma dzanja la akhama lilemeretsa.
5. Wokolola m'malimwe ndi mwana wanzeru;Koma wogona pakututa ndi mwana wocititsa manyazi.
6. Madalitso ali pamtu pa wolungamaKoma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.
7. Amayesa wolungama wodala pamkumbukira;Koma dzina la oipa lidzabvunda.
8. Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;Koma citsiru colongolola cidzagwa.
9. Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;Koma wokhotetsa njira zace adzadziwika.
10. Wotsinzinira acititsa cisoni;Koma wodzudzula momveka acita mtendere.
11. M'kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;Koma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.