28. Ciyembekezo ca olungama ndico cimwemwe;Koma cidikiro ca oipa cidzaonongeka.
29. Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima;Koma akucita zoipa adzaonongeka.
30. Wolungama sadzacotsedwa konse:Koma oipa sadzakhalabe m'dziko.
31. M'kamwa mwa wolungama mulankhula nzeru;Koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32. Milomo ya wolungama idziwa zokondweretsa;Koma m'kamwa mwa oipa munena zokhota,