Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 10:28-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ciyembekezo ca olungama ndico cimwemwe;Koma cidikiro ca oipa cidzaonongeka.

29. Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima;Koma akucita zoipa adzaonongeka.

30. Wolungama sadzacotsedwa konse:Koma oipa sadzakhalabe m'dziko.

31. M'kamwa mwa wolungama mulankhula nzeru;Koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32. Milomo ya wolungama idziwa zokondweretsa;Koma m'kamwa mwa oipa munena zokhota,

Werengani mutu wathunthu Miyambi 10