Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 10:12-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Udani upikisanitsa;Koma cikondi cikwirira zolakwa zonse.

13. Nzeru ipezedwa m'milomo ya wozindikira;Koma wopusa pamsana pace ntyole.

14. Anzeru akundika zomwe adziwaKoma m'kamwa mwa citsiru muononga tsopano lino.

15. Cuma ca wolemera ndi mudzi wace wolimba;Koma umphawi wao uononga osauka.

16. Nchito za wolungama zipatsa moyo;Koma phindu la oipa licimwitsa.

17. Wosunga mwambo ali m'njira ya moyo;Koma wosiya cidzudzulo asocera.

18. Wobisa udani ali ndi milomo yonama;Wonena ugogodi ndiye citsiru.

19. Pocuruka mau zolakwa sizisoweka;Koma wokhala cete acita mwanzeru.

20. Lilime la wolungama likunga siliva wosankhika;Koma mtima wa oipa uli wacabe.

21. Milomo ya wolungama imadyetsa ambiri;Koma zitsiru zimafa posowa nzeru.

22. Madalitso a Yehova alemeretsa,Saonjezerapo cisoni.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 10