Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 10:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwana wanzeru akondweretsa atate;Koma mwana wopusa amvetsa amace cisoni.

2. Cuma ca ucimo sicithangata:Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.

3. Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama;Koma amainga cifuniro ca wocimwa.

4. Wocita ndi dzanja laulesi amasauka;Koma dzanja la akhama lilemeretsa.

5. Wokolola m'malimwe ndi mwana wanzeru;Koma wogona pakututa ndi mwana wocititsa manyazi.

6. Madalitso ali pamtu pa wolungamaKoma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.

7. Amayesa wolungama wodala pamkumbukira;Koma dzina la oipa lidzabvunda.

8. Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;Koma citsiru colongolola cidzagwa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 10