Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mika 1:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Musacifotokoza m'Gati, musalira misozi konse; m'nyumba ya Afira ndinagubuduka m'pfumbi.

11. Pitiratu, wokhala m'Safiri iwe, wamarisece ndi wamanyazi; wokhala m'Zanana sanaturuka; maliro a Betezeli adzakulandani pokhala pace.

12. Pakuti wokhala m'Maroti alindira cokoma, popeza coipa catsika kwa Yehova kumka ku cipata ca Yerusalemu.

13. Manga gareta ku kavalo waliwiro, wokhala m'Lakisi iwe, woyamba kucimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni ndi iye; pakuti zolakwa za Israyeli zinapezedwa mwa iwe.

14. Cifukwa cace pereka mphatso zolawirana kwa Moreseti Gati; nyumba za Akizibi zidzakhala cinthu cabodza kwa mafumu a Israyeli.

15. Ndidzakutengeranso wokhala m'Maresa iwe, iye amene adzakulandira ukhale colowa cace; ulemerero wa Israyeli udzafikira ku Adulamu.

Werengani mutu wathunthu Mika 1