Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 97:6-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Kumwamba kulalikira cilungamo cace,Ndipo mitundu yonse ya anthu ipenya ulemerero wace.

7. Onse akutumikira fano losema,Akudzitamandira nao mafano, acite manyazi:Mgwadireni Iye, milungu yonse inu.

8. Ziyoni anamva nakondwera,Nasekerera ana akazi a Yuda;Cifukwa ca maweruzo anu, Yehova.

9. Pakuti Inu, Yehova, ndinu Wam'mwambamwamba pa dziko lonse lapansi,Ndinu wokwezeka kwakukuru pamwamba pa milungu yonse yina.

10. Inuokonda Yehova, danani naco coipa:Iye asunga moyo wa okondedwa ace;Awalanditsa m'manja mwa oipa.

11. Kuunika kufesekera wolungama, Ndi cikondwerero oongoka mtima.

12. Kondwerani mwa Yehova, olungama inu;Ndipo yamikani pokumbukila ciyero cace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 97