Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 97:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yehova acita ufumu; dziko lapansi likondwere;Zisumbu zambiri zikondwerere.

2. Pomzinga pali mitambo ndi mdima;Cilungamo ndi ciweruzo ndizo zolimbitsa mpando wacifumu wace.

3. Moto umtsogolera,Nupsereza otsutsana naye pozungulirapo,

4. Mphezi zace zinaunikira dziko lokhalamo anthu;Dziko lapansi linaona nilinagwedezeka.

5. Mapiri anasungunuka ngati sera pamaso pa Yehova,Pamaso pa Ambuye wa dziko lonse lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 97