8. Yehova, Mulungu wa makamu, wamphamvu ndani wonga Inu, Yehova?Ndipo cikhulupiriko canu cikuzingani.
9. Inu ndinu wakucita ufumu pa kudzikuza kwa nyanja;Pakuuka mafunde ace muwacititsa bata.
10. Mudathyola Rahabu, monga munthu wophedwa;Munabalalitsa adani anu ndi mkono wa mphamvu yanu.
11. Kumwamba ndi kwanu, dziko lapansi lomwe ndi lanu;Munakhazika dziko lokhalamo anthu ndi kudzala kwace.
12. Munalenga kumpoto ndi kumwela;Tabora ndi Hermoni apfuula mokondwera m'dzina lanu.
13. Muli nao mkono wanu wolimba;M'dzanja mwanu muli mphamvu, dzanja lamanja lanu nlokwezeka.
14. Cilungamo ndi ciweruzo ndiwo maziko a mpando wacifumu wanu;Cifundo ndi coonadi zitsogolera pankhope panu.
15. Odala anthu odziwa liu la lipenga;Ayenda m'kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.
16. Akondwera m'dzina lanu tsiku lonse;Ndipo akwezeka m'cilungamo canu.
17. Popeza Inu ndinu ulemerero wa mphamvu yao;Ndipo potibvomereza Inu nyanga yathu idzakwezeka.
18. Pakuti cikopa cathu cifuma kwa Yehova;Ndi mfumuyathu kwa Woyera wa Israyeli.
19. Pamenepo munalankhula m'masompenya ndi okondedwa anu,Ndipo mudati, Ndasenza thandizo pa ciphona;Ndakweza wina wosankhika mwa anthu.
20. Ndapeza Davide mtumiki wanga;Ndamdzoza mafuta anga oyera.
21. Amene dzanja langa lidzakhazikika naye;Inde mkono wanga udzalimbitsa.