49. Ciri kuti cifundo canu cakale, Ambuye,Munacilumbirira Davide pa cikhulupiriko canu?
50. Kumbukilani, Ambuye, cotonzera atumiki anu;Ndicisenza m'cifuwa mwanga cacokera ku mitundu yonse yaikuru ya anthu;
51. Cimene adani anu, Yehova, atonza naco;Cimene atonzera naco mayendedwe a wodzozedwa wanu.
52. Wodalitsika Yehova ku nthawi yonse,Amen ndi Amen.