Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 89:47-52 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

47. Kumbukilani kuti nthawi yanga njapafupi;Munalengeranji ana onse a anthu kwacabe?

48. Munthu ndani amene adzakhalabe ndi moyo, osaona imfa?Amene adzapulumutsa moyo wace ku mphamvu ya manda?

49. Ciri kuti cifundo canu cakale, Ambuye,Munacilumbirira Davide pa cikhulupiriko canu?

50. Kumbukilani, Ambuye, cotonzera atumiki anu;Ndicisenza m'cifuwa mwanga cacokera ku mitundu yonse yaikuru ya anthu;

51. Cimene adani anu, Yehova, atonza naco;Cimene atonzera naco mayendedwe a wodzozedwa wanu.

52. Wodalitsika Yehova ku nthawi yonse,Amen ndi Amen.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 89