Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 89:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndidzakhazika mbeu yako ku nthawi yonse,Ndipo ndidzamanga mpando wacifumu wako ku mibadwo mibadwo.

5. Ndipo kumwamba kudzalemekeza zodabwiza zanu, Yehova;Cikhulupiriko canunso mu msonkhano wa oyera mtima.

6. Pakuti kuli yani kuthambo timlinganize ndi Yehova?Afanana ndi Yehova ndani mwa ana a amphamvu?

7. Ndiye Mulungu, ayenera kumuopa kwambiri m'upo wa oyera mtima,Ndiye wocititsa mantha koposa onse akumzinga.

8. Yehova, Mulungu wa makamu, wamphamvu ndani wonga Inu, Yehova?Ndipo cikhulupiriko canu cikuzingani.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 89