39. Munakaniza cipangano ca mtumiki wanu;Munaipsa korona wace ndi kumponya pansi,
40. Munapasula maguta ace onse;Munagumula malinga ace.
41. Onse opita panjirapa amfunkhira:Akhala cotonza ca anansi ace.
42. Munakweza dzanja lamanja la iwo omsautsa;Munakondweretsa adani ace onse.
43. Munapinditsa kukamwa kwace kwa lupanga lace,Osamuimika kunkhondo.
44. Munaleketsa kuwala kwace,Ndipo munagwetsa pansi mpando wacifumu wace.
45. Munafupikitsa masiku a mnyamata wace;Munamkuta nao manyazi.
46. Mudzabisala kosatha kufikira liti, Yehova;Ndi kuzaza kwanu kudzatentha ngati moto kufikira liti?
47. Kumbukilani kuti nthawi yanga njapafupi;Munalengeranji ana onse a anthu kwacabe?
48. Munthu ndani amene adzakhalabe ndi moyo, osaona imfa?Amene adzapulumutsa moyo wace ku mphamvu ya manda?
49. Ciri kuti cifundo canu cakale, Ambuye,Munacilumbirira Davide pa cikhulupiriko canu?