Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 89:39-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Munakaniza cipangano ca mtumiki wanu;Munaipsa korona wace ndi kumponya pansi,

40. Munapasula maguta ace onse;Munagumula malinga ace.

41. Onse opita panjirapa amfunkhira:Akhala cotonza ca anansi ace.

42. Munakweza dzanja lamanja la iwo omsautsa;Munakondweretsa adani ace onse.

43. Munapinditsa kukamwa kwace kwa lupanga lace,Osamuimika kunkhondo.

44. Munaleketsa kuwala kwace,Ndipo munagwetsa pansi mpando wacifumu wace.

45. Munafupikitsa masiku a mnyamata wace;Munamkuta nao manyazi.

46. Mudzabisala kosatha kufikira liti, Yehova;Ndi kuzaza kwanu kudzatentha ngati moto kufikira liti?

47. Kumbukilani kuti nthawi yanga njapafupi;Munalengeranji ana onse a anthu kwacabe?

Werengani mutu wathunthu Masalmo 89