Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 89:28-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ndidzamsungira cifundo canga ku nthawi yonse,Ndipo cipangano canga cidzalimbika pa iye.

29. Ndidzakhalitsanso mbeu yace cikhalire,Ndi mpando wacifumu wace ngati masiku a m'mwamba.

30. Ana ace akataya cilamulo canga,Osayenda m'maweruzo anga:

31. Nakaipsa malembo anga;Osasunga malamulo anga;

32. Pamenepo ndidzazonda zolakwa zao ndi ndodo,Ndi mphulupulu zao ndi mikwingwirima.

33. Koma sindidzamcotsera cifundo canga conse,Ndi cikhulupiriko canga sicidzamsowa.

34. Sindidzaipsa cipangano canga,Kapena kusintha mau oturuka m'milomo yanga.

35. Ndinalumbira kamodzi m'ciyero canga;Sindidzanamizira Davide;

36. Mbeu yace idzakhala ku nthawi yonse,Ndi mpando wacifumu wace ngati dzuwa pamaso panga.

37. Udzakhazikika ngati mwezi ku nthawi yonse,Ndi ngati mboni yokhulupirika kuthambo.

38. Koma Inu munamtaya, nimunamkaniza,Munakwiya naye wodzozedwa wanu.

39. Munakaniza cipangano ca mtumiki wanu;Munaipsa korona wace ndi kumponya pansi,

40. Munapasula maguta ace onse;Munagumula malinga ace.

41. Onse opita panjirapa amfunkhira:Akhala cotonza ca anansi ace.

42. Munakweza dzanja lamanja la iwo omsautsa;Munakondweretsa adani ace onse.

43. Munapinditsa kukamwa kwace kwa lupanga lace,Osamuimika kunkhondo.

44. Munaleketsa kuwala kwace,Ndipo munagwetsa pansi mpando wacifumu wace.

45. Munafupikitsa masiku a mnyamata wace;Munamkuta nao manyazi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 89